Back to top

Sabbath Bible Lessons

Uthenga Wabwino Malinga ndi Yohane (GA WO LACHIWIRI)

 <<    >> 
PHUNZIRO 5 SABATA, MEYI 3, 2025

“NGAKHALE INENSO SINDIKUTSUTSA IWE”

VESI LOLOWEZA: “Inenso sindikutsutsa iwe; pita; kuyambira tsopano usachimwenso” (Yohane 8:11, mbali yomalidza).

“Chikondi chachikhristu chimakhala chochedwa kutsutsa, chimakhala chachangu kuzindikira kugonja, chokonzeka kukhululukira, kulimbikitsa, kukhazikitsa osochera munjira ya chiyero, ndikuwakhazikitsa mapazi awo mmenemo”- The Desire of Ages, p. 462.

Zowelenga zoonjezera:   Testimonies for the Church, vol 2, pp. 73-77. 

Loyamba , Epulo 27

1. MSAMPHA WA YESU

a. Pamene Yesu anali kuphuzitsa mkachisi, kodi ndi chiyani chimene Alembi ndi Afalisi anachita? Yohane 8:2-3.

“(Khristu) mwachangu anasokonezedwa. Gulu la Afalisi ndi Alembi linaza kwa iye, likukoka mzimayi wogwidwa ndi mantha, amene ndimawu okuwa komanso olimba iwo amamuneneza iye zakuphwanya lamulo lachisanu ndi chiwiri.”- The Desire of Ages, p. 460.

b. Ponetsera ulemu wooneka waukulu wa malamulo, kodi ndi funso lanji limene Afalisi analipeleka kwa Khristu-nanga kodi cholinga chawo chenicheni chinali chiyani? Yohane 8:4- 6(Mbali yoyamba).

“Kulemekeza kwawo kwachinyengo kunaphimba dongosolo lawo lakuya limene anakhazikitsa kuchionongeko chake. Iwo anatenga mwayi umenewu kuti akhazikitse chiweludzo chakumutsutsa iye, poganiza kuti yankho lililonse limene iye angathe kulipereka, iwo adzapeza mwayi wakumuneneza iye. Ngati iye angamukhululukire mzimayiyo, ndiye kuti iye atha kuimbidwa mulandu wakupeputsa lamulo la Mose. Ngati iye angamuweludze iye kuti ndiwoyenera kuphedwa, iye adzanenezedwa kwa Aroma monga mmodzi amene akuzipatsa ulamuliro umene ndi waiwo okha basi.”- Ibid., pp. 460, 461.


Lachiwiri , Epulo 28

2. CHITHUNZITHUNZI CHENICHENI CHIBVUNDUKULIDWA

a. Kodi ndimotani mmene Yesu anayankhira kuchinyengo cha Afalisi? Yohane 8:6(mbali yomaliza).

“Yesu anayang’ana kwakamphindi pazochitikazi- pa olakwa onjenjemera mumanyazi ake, pankhope zopanda chisoni za olemekezeka, zopandilatu ingakhale chisoni chaumunthu. Mzimu wake wachiyero chopanda banga unakhuzika pakuona zotelezi. Iye bwinobwino amadziwa cholinga chimene mlanduwu wabweletsedwa kwa Iye. Iye amawerenga mtima, ndikuziwa khalidwe ndi mbili ya moyo wawina aliyense amene anali pamaso pake. Awawa ozinena kukhala oteteza chilungamo akhala akutsogolera olakwayi kuuchimo, kotelo kuti iwo akathe kuchela msampha Yesu. Popanda kuonetsa chizindikiro china chilichonse cha kuti iye wamva funso lawo, Iye anawelama pansi, nakhazikitsa maso ake pansi, ndipo anayamba kulemba pansi.”-The Desire of Ages, p. 461.

b. Kodi ndimotani mmene Yesu anaonetsera kuti onenezawo iwo eni sianthu oti alibe chimo- nanga ndichiyani chimene iwo anachita kenako? Yohane 8:7-9.

“Oneneza anagonjesedwa. Tsopano, mikanjo yawo yachiyero chonamizira inang’ambidwa kuchoka kwa iwo,iwo anayima, otsutsidwa ndi ochimwa, pamaso pa olungama wamuyaya. Iwo ananjenjemera kuopa kuti zochimwa zawo zobisika zammiyoyo yawo zitha kuikidwa poyela pamaso pa khamu laanthu; ndipo mmodzimodzi wa iwo, ndinkhope zakugwa ndimaso oyang’ana pansi, anachoka pamalopa, ndikusiya munthu olakwa wawo limodzi ndi mpulumutsi wachisoni.” – Ibid.

c. Muchina chili chonse, Kodi ndi chiyani chimene ife tonse tikuyenera kuphunzira kuchokela kumawu a Yesu kwa oneneza? Luka 6:42.

“Pali anthu amene ali osakhwima mukhumbo lawo lakukonzanso zinthu zimene kwa iwo zimaoneka zolakwika. Iwo amaganiza kuti iwo akuyenera kusankhidwa kuti atenge malo aiwo amene apanga zophophonya. Iwo amapeputsa zimene ogwira ntchito amenewa anachita pamene ena amangoyang’ana ndikutsutsa moweludza. Kudzera mmachitidwe awo iwo amati, ‘Ndingathe ine kuchita zinthu zazikulu. Ndingathe ine kupititsa ntchito patsogolo ndichipambano.’ Kwa iwo amene amaganiza kuti akuziwa bwino kwambiri mmene angapewele zolakwitsa, ine ndinalamulilidwa kuti ndinene kuti, ‘musaweludze,kuti mungaweluzidwe.’ Mateyu 7:1. Inu mungathe kupewa zolakwitsa muzinthu zina, koma muzinthu zina muli ndikuthekera inu kwakupanga zolakwika zazikulu kwambiri, zimene zizakhala zovuta kwambiri kuzikonza ndipo zimene zizabweretsa chisokonezo muutumiki. Zophophonya zimenezi zizatha kuononga kwambiri kupotsera izo zimene abale anu anachita.”-Testimonies for the Church, vol. 7, p. 279.


Lachitatu , Epulo 29

3. CHOCHITIKA CHOSAYEMBEKEZELEKA

a. Kodi ndifunso lanji limene Yesu anamufunsa Mzimayi atatha kuchoka omuneneza ake-nanga ndimotani mmene njira yake ya kuchitila ndi nkhaniyi ingakakhuzire moyo wake wa mzimayiyu? Yohane 8:10, 11.

“Mzimayi anaima pamaso pa Yesu, odzazidwa ndimantha. Mawu ake oti, ‘iye amene mwainu ali opanda chimo, ayambe kumponya mwala,’ Anabwela kwa iye ngati chigamulo cha imfa. Iye sanayelekeze kutukula maso ake kuyang’ana nkhope ya Mpulumutsi, Koma mwakachetechete anayembekezera imfa yake. Modabwa iye anaona omuneneza ake akuchoka opanda mawu ndi okhazikitsidwa chete; kenako mau achiyembekezo anafika mmakutu ake,`inenso sindikutsutsa iwe; pita; kuyambila tsopano usachimwenso.’ Mtima wake unasukunulidwa, ndipo, ndi pozigwetsa yekha pamapazi a Yesu, iye analira ndichikondi chake chachiyamiko ndimisozi yowawidwa mtima anavomeleza machimo ake.

“Ichi kwa iye chinali chiyambi cha moyo watsopano, moyo wachiyelo ndi mtendele, wozipereka kwa Mulungu. Mukukweza kwa moyo wakugwa umenewu, Yesu anachita chozizwa chachikulu kwambiri kupotsera kuchilitsa nthenda yaikulu kwambiri yakuthupi; iye anachilitsa nthenda yauzimu imene ili yofikila kuimfa yamuyaya. Mzimayi wolapayu anakhala mmodzi waotsatira ake ozipereka kwambiri. Ndi chikondi chozipereka yekha nsembe iye anaonetsera chiyamiko chake pachifundo chake chakukhululukira. Kwa mzimayi olakwitsayu dziko linali ndi chiweluzo ndi kunyoza basi, koma Osalakwayo anamvera chisoni kufooka kwake ndipo anamuyandikira iye ndikumutambasulira dzanja la chithangato. Amene Afalisi achinyengo anatsutsa, Yesu anamulamulira iye kuti, `pita, kuyambira tsopano usakachimwenso.’”- The Ministry of Healing, p. 89.

“Mumchitidwe wake wakukhululukira mzimayiyu ndikumulimbikitsa iye kuti akhale moyo wabwino, khalidwe la Yesu linawala ponseponse mukukongola kwa chilungamo chodzadza. Pamene Iye sabvomeleza chimo, kapena kuchepetsa kuipa kwachimo, iye amafunitsitsa osati kususa, koma kupulumutsa. Kwa mzimayi wolakwayu dziko linali ndi kusutsa ndi kunyodza basi; koma Yesu akuyankhula mawu achitonthozo ndi chiyembekezo.”- The Desire of Ages, p. 462

b. Fotokozani zotsatira zachisomo chopulumutsa cha Khristu. Luka 7:37-40, 47, 48.

“Yesu amadziwa zochitikachitika zamoyo winaulionse. Monga Kukula kwa kuipisisa kwa ochimwa momwemonso ndi momwe amafunira mpulumutsi. Mtima wake wachikondi ndi chisoni cha Umulungu ukukoka koposa wina aliyense iye amene ndiosowelatu thandizo ogwidwa mmisampha ya mdani. Ndimwazi wa iye yekha iye anasindikiza chizindikiro pamapepala akumasula mtundu waanthu.”-The Ministry of Healing, pp. 89–90.


Lachinayi , Epulo 30

4. CHITONTHOZO CHIFALIKILA PONSEPONSE

a. Kodi khalidwe lathu likuyenera kukhala lotani, makamaka pochita ndi ena-nanga kodi izizi zingatheke bwanji kokha? 2 Akolinto 1:3-5

“Zochitikachitika zili ndi gawo lochepa chabe mokhuzana ndi zodusamo za moyo. Ndi mzimu umene umakondwereredwa umene umakongoletsa machitidwe athu onse. Munthu amene ali pamtendere ndi Mulungu komanso ndi anthu anzake sangakhumudwitsike. Msanje sizakhala mumtima mwake; zoneneza zoipa sizizapeza malo mmenemo; udani sungakhalepo. Mtima umene uli mumgwirizano ndi Mulungu umakwezedwa pamwamba pa zokhumudwitsa ndi mayesero a moyo uno.”-Testimonies for the Church, vol. 5, p. 488.

“Ndikudzera mmasautso kuti Yesu anapedza utumiki wachitonthodzo. Mumasautso onse aumunthu iye amasautsika; Ndipo ‘madzunzo awo onse iye anazunzidwa,pakuti popeza ananva zowawa poyesedwa yekha, akhoza kuthandiza iwo amene ayesedwa.’ Yesaya 63:9; Ahebri 2:18. Muutumiki uwu moyo ulionse umene walowa muchiyanjano chamatsautso ake uli ndi mwayi wakugawana nawo.” -Thought from the Mount of Blessings, p. 13.

b. Fotokozani mwayi ndi chiyembekezo chapadela chimene ife tili nacho mukusatira mapazi a Khristu. 2 Akolinto 1:6, 7.

“Ngati inu simuzinva mumtima mwanu kuti anakulemekezani kuti mukhale otenga nawo gawo a masautso a Khristu; Ngati simuchinva kukhala cholemetsa chamoyo cha zaiwo amene ndiokonzeka kuonongeka; ngati inu simuli ofuna kupereka nsembe kuti mukathe kusunga chuma cha ntchito imene iyenera kuti igwiridwe, sikumuzakhala malo anu muufumu wa Mulungu. Tikufunika ife kukhala otenga nawo mbali ndi Khristu a masautso ake ndikuzikaniza wekha kwake pakhwerero lina lililonse.”- Tetsimonies for the Church, vol. 9, pp. 103, 104.

c. Fotokozani khalidwe labwino limene likufunikira kwambiri pakati pa okhulupilira muuthenga wa angelo atatu. 1 Akolinto 13:13,4-8

“Makhalidwe amene akufunikira kwambiri kuti azikuzidwa ndi anthu a Mulungu osunga malamulo ndi chipiliro ndi kuledza mtima, mtendere ndi chikondi. Pamene chikondi chikusowa, kuludza kwakukulu kumachitika.”- Ibid., vol. 6, p. 398.


Lachisanu , Meyi 1

5. KUBWEZELETSA KWA CHIFUNDO

a. Kodi ndimotani mmene okhulupirira owona amachitila ngati mkhristu wagwera muuchimo-mosiyana ndi mmene okhulupilira amitima yonyenga kawirikawiri amachitira? Agalatiya 6:1-3; Aroma 15:1-3.

“Chiikeni mumtima mwanu kuti ntchito yakubwezeretsa ikuyenera kukhala cholemetsa chathu. Ntchito imeneyi siikuyenera kuchitidwa munjira yonyada, yozikweza, yaulamuliro. Musamanene inu, kudzera mmachitidwe anu kuti, ‘ndili ndi mphanvu, ndipo ine ndizigwiritsa ntchito zimenezo,’ ndikumafotokoza zoneneza zambirimbiri kwa munthu wolakwitsayo. Gwirani ntchito yanu yakubwezeretsa `Muuzimu wachifatso; ndikuzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.’ Ntchito imene tapatsidwa ife kuti tiigwire kwa abale athu sikuwachotsa iwo ndikuwaika pambali, osati kuwapanikizira iwo kupita kukugwetsedwa mphwayi kapena kukukhumudwa kudzera mukumanena kuti.. ‘Inu mwandikhumudwitsa ine, ndipo sindiyetsa kukuthandizani inu’ Iye amene amazikweza yekha pamwamba ngati ozaza ndi mzeru ndi mphanvu, ndikumapepusa iye amene waphinjika ndikukhala ndi nkhawa ndikumafunitsitsa thandizo, akuonetsera mzimu wa mfalisi, ndipo wazitsokera yekha mwinjiro wakulemekezeka kozipangira yekha. Muuzimu wake iye amathokoza Mulungu kuti sali ngati anthu ena, ndipo amaganiza kuti machitidwe ake ndioyamikilidwa kwambiri ndikuti iye ndiwamphanvu kwambiri kuti angayetsedwe. Koma `Ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali chabe, azinyenga yekha.’ vesi 3.”-Testimonies for the Church, vol. 6, pp. 398–399.

“Siotsatira Khristu amene, ndimaso otseka mwadala, amatembenuka kuchoka kwa olakwitsa, kuwatsiya iwo osawatsokonedza kuti atsatire njira yawo yopita pansi kuchionongeko. Iwo amene amakhala patsogolo mukuneneza ena, ndikukhala achangu mukuwabweretsa iwo muchiweludzo, kawirikawiri mmiyoyo yawo amakhala olakwa kwambiri koposa iwo aja. Anthu amadana ndi ochimwa, pamene iwo akukonda uchimo. Khristu amadana ndi uchimo, koma amakonda ochimwa. Uwu udzakhala mzimu waonse amene amamutsatira iye. Chikondi cha chikhristu ndichochedwa kutsutsa, chachangu kuzindikira kulapa, chokonzeka kukhululukira, kulimbikitsa, kukhazikitsa osochera munjira yachiyero, ndikukhazikitsa mapazi ake mmenemo.” - The Desire of Ages, p. 462.


Lachisanu ndi chimodzi , Meyi 2

6. MAFUNSO OBWEREZA PAWEKHA

1. Fotokozani msampha umene Alembi ndi Afalisi anamukonzera khristu.

2. Kodi ndimotani mmene Ayuda achinyengo anaonetsera kulemekedza kwabodza lamulo?

3. Kodi ndichiyani chimene Ayuda oneneza anakakamizidwa kuti avomeleze zokhuza iwo eni?

4. Fotokozani chiyembekezo chimene chinaperekedwa kwa mzimayi olakwa amene amachitidwa moyipa.

5. Kodi ndimotani mmene ine ndingakhalire monga Yesu pamene ndikuchita ndi moyo wolakwa?

 <<    >>